Mateyu 21:5-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Tauzani mwanawamkazi wa Ziyoni,Taona, Mfumu yako idza kwa iwe,Wofatsa ndi wokwera pa buru,Ndi pa kaburu, mwana wa nyama yonyarnula katundu.

6. Ndipo ophunzirawo anamuka, nacita monga Yesu anawauza;

7. nabwera ndi buru ndi mwana wace, naika pa iwo zobvala zao, nakhala Iye pamenepo.

8. Ndipo ambirimbiri a mpingowo anayala zobvala zao panjira; Ndipo ena anadula nthambi za mitengo, naziyala m'njirarno.

Mateyu 21