Mateyu 2:21-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo anauka iye, natenga kamwana ndi amace, nalowa m'dziko la Israyeli.

22. Koma pakumva iye kuti Arikelao anali mfumu ya Yudeya m'malo mwa atate wace Herode, anacita mantha kupita kumeneko; ndipo pamene anacenjezedwa ndi Mulungu m'kulota, anamuka nalowa ku dziko la Galileya,

23. nadza nakhazikika m'mudzi dzina lace Nazarete kuti cikacitidwe conenedwa ndi aneneri kuti, Adzachedwa Mnazarayo.

Mateyu 2