Mateyu 16:4-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Obadwa oipa ndi acigololo afunafuna cizindikiro; ndipo sadzalandira cizindikiro cina, koma cizindikiro ca Yona. Ndipo Iye anawasiya, nacokapo.

5. Ndipo ophunzira anadza ku tsidya linalo, naiwala kutenga mikate.

6. Ndipo Yesu anati kwa iwo, Yang'anirani mupewe cotupitsa mkate ca Afarisi ndi Asaduki.

7. Ndipo iwo anafunsana wina ndi mnzace, nati, Sitinatenga mikate.

8. Koma Yesu, m'mene anadziwa, anati, Ha, inu okhulupirira pang'ono, mufunsana cifukwa ninji wina ndi mnzace, kuti simunatenga mikate?

9. kodi cikhalire simudziwa, ndipo simukumbukira mikate isanu ija ya anthu aja zikwi zisanu, ndi mitanga ingati munaitola?

10. Penanso mikate isanu ndi iwiri ija ya anthu zikwi zinai, ndi malicero angati munawatola?

11. Bwanji nanga simudziwa kuti sindinanena kwa inu za mikate? Koma pewani cotupitsa ca Afarisi ndi Asaduki.

12. Pomwepo anadziwitsa kuti sanawauza kupewa cotupitsa ca mikate, koma ciphunzitso ca Afarisi ndi Asaduki.

Mateyu 16