Mateyu 15:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Onyenga inu! Yesaya ananenera bwino za inu, ndikuti,

8. Anthu awa andilemekeza Ine ndi milomo yao;Koma mtima wao uli kutari ndi Ine.

9. Koma andilambira Ine kwacabe,Ndi kuphunzitsa maphunzitso, malangizo a anthu.

10. Ndipo Iye anaitana makamuwo nati kwa iwo, Imvani, nimudziwitse;

11. si cimene cilowa m'kamwa mwace ciipitsa munthu; koma cimene cituruka m'kamwa mwace, ndico ciipitsa munthu.

12. Pomwepo anadza ophunzira, nanena kwa Iye, Mudziwa kodi kuti Afarisi anakhumudwa pakumva conenaco?

Mateyu 15