Mateyu 14:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Pomwepo iye anamlonjeza cilumbirire, kumpatsa iye cimene ciri conse akapempha.

8. Ndipo iye, atampangira amace, anati, Ndipatseni ine kuno m'mbizi mutu wa Yohane Mbatizi. Ndipo mfumuyo anagwidwa ndi cisoni;

9. koma cifukwa ca malumbiro ace, ndi ca iwo anali naye pacakudya, analamulira upatsidwe;

10. ndipo anatumiza mnyamata, namdula mutu Yohane m'nyumba yandende.

Mateyu 14