7. Pomwepo iye anamlonjeza cilumbirire, kumpatsa iye cimene ciri conse akapempha.
8. Ndipo iye, atampangira amace, anati, Ndipatseni ine kuno m'mbizi mutu wa Yohane Mbatizi. Ndipo mfumuyo anagwidwa ndi cisoni;
9. koma cifukwa ca malumbiro ace, ndi ca iwo anali naye pacakudya, analamulira upatsidwe;
10. ndipo anatumiza mnyamata, namdula mutu Yohane m'nyumba yandende.