1. Nthawi imeneyo Herode mfumu anamva mbiri ya Yesu,
2. nanena kwa anyamata ace, U yo ndiye Yohane Mbatizi; anauka kwa akufa; ndipo cifukwa ca ici zamphamvuzi zilimbalimba mwa iye.
3. Pakuti Herode adamgwira Yohane, nammanga, namuika m'nyumba yandende cifukwa ca Herodiya, mkazi wa mbale wace Filipo.
4. Pakuti Yohane ananena kwa iye, Sikuloledwa kwa iwe kukhala naye.
5. Ndipo pofuna kumupha iye, anaopa khamu la anthu, popeza anamuyesa iye mneneri.