16. Koma maso anu ali odala, cifukwa apenya; ndi makutu anu cifukwa amva.
17. Pakuti indetu ndinena kwa inu, kuti aneneri ambiri ndi anthu olungama analakalaka kupenya zimene muziona, koma sanaziona; ndi kumva zimene muzimva, koma sanazimva.
18. Ndipo tsono mverani inu fanizolo la wofesa mbeu uja.