Mateyu 11:26-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. etu, Atate, cifukwa cotero cinakhala cokondweretsa pamaso panu.

27. Zinthu zonse zinaperekedwa kwa Ine ndi Atate wanga; ndipo palibe munthu adziwa Mwana, koma Atate yekha; ndi palibe wina adziwa Atate, koma M wana yekha, ndi iye amene Mwana afuna kumuululira.

28. Idzani kuno kwa Ine nonsenu akulema ndi akuthodwa, ndipo Ine ndidzakupumulitsani inu.

29. Senzani gori langa, ndipo phunzirani kwa Ine; cifukwa ndiri wofatsa ndi wodzicepetsa mtima: ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu.

30. Pakuti 1 gori langa liri lofewa, ndi katundu wanga ali wopepuka.

Mateyu 11