4. Simoni Mkanani, ndi Yudasi Isikariote amenenso anampereka Iye.
5. Awa amene, khumi ndi awiriwa, Yesu anawatumiza, nawalangiza ndi kuti,Musapite ku njira ya kwa anthu akunja, ndi m'mudzi wa Asamariya musamalowamo:
6. koma makamaka mupite ku nkhosa zosokera za banja la Israyeli.
7. Ndipo pamene mulikupita lalikani kuti, Ufumu wa Kumwamba wayandikira.
8. Ciritsani akudwala, ukitsani akufa, konzani akhate, turutsani ziwanda: munalandira kwaulere, patsani kwaulere.
9. Musadzitengere ndalama zagolidi, kapena zasiliva, kapena zakobiri m'malamba mwanu;