Mateyu 10:4-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Simoni Mkanani, ndi Yudasi Isikariote amenenso anampereka Iye.

5. Awa amene, khumi ndi awiriwa, Yesu anawatumiza, nawalangiza ndi kuti,Musapite ku njira ya kwa anthu akunja, ndi m'mudzi wa Asamariya musamalowamo:

6. koma makamaka mupite ku nkhosa zosokera za banja la Israyeli.

7. Ndipo pamene mulikupita lalikani kuti, Ufumu wa Kumwamba wayandikira.

8. Ciritsani akudwala, ukitsani akufa, konzani akhate, turutsani ziwanda: munalandira kwaulere, patsani kwaulere.

9. Musadzitengere ndalama zagolidi, kapena zasiliva, kapena zakobiri m'malamba mwanu;

Mateyu 10