Masalmo 94:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mulungu wakubwezera cilango,Yehova, Mulungu wakubwezera cilango, muoneke wowala.

2. Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi:Bwezerani odzikuza coyenera iwo.

3. Oipa adzatumpha ndi cimwemwe kufikira liti, Yehova?Oipa adzatero kufikira liti?

4. Anena mau, alankhula zawawa;Adzitamandira onse ocita zopanda pace.

5. Aphwanya anthu anu, Yehova,Nazunza colandira canu.

6. Amapha wamasiye ndi mlendo,Nawapha ana amasiye.

7. Ndipo amati, Yehova sacipenya,Ndi Mulungu wa Yakobo sacisamalira.

Masalmo 94