4. Popeza Inu, Yehova, munandikondweretsa ndi kucita kwanu,Ndidzapfuula mokondwera pa nchito ya manja anu.
5. Ha! nchito zanu nzazikuru, Yehova,Zolingalira zanu nzozama ndithu.
6. Munthu wopulukira sacidziwa;Ndi munthu wopusa sacizindikira ici;
7. Cakuti pophuka oipa ngati msipu,Ndi popindula ocita zopanda pace;Citero kuti adzaonongeke kosatha: