4. Adzakufungatira ndi nthenga zace,Ndipo udzathawira kunsi kwa mapiko ace;Coonadi cace ndico cikopa cocinjiriza.
5. Sudzaopa coopsa ca usiku, Kapena mubvi wopita usana;
6. Kapena mliri woyenda mumdima,Kapena cionongeko cakuthera usana.
7. Pambali pako padzagwa cikwi,Ndi zikwi khumi pa dzanja lamanja lako;Sicidzakuyandikiza iwe.