Masalmo 91:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Adzakufungatira ndi nthenga zace,Ndipo udzathawira kunsi kwa mapiko ace;Coonadi cace ndico cikopa cocinjiriza.

5. Sudzaopa coopsa ca usiku, Kapena mubvi wopita usana;

6. Kapena mliri woyenda mumdima,Kapena cionongeko cakuthera usana.

7. Pambali pako padzagwa cikwi,Ndi zikwi khumi pa dzanja lamanja lako;Sicidzakuyandikiza iwe.

Masalmo 91