Masalmo 90:2-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Asanabadwe mapiri,Kapena musanalenge dziko lapansi, ndi lokhalamo anthu,Inde, kuyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha,Inu ndinu Mulungu.

3. Mubweza munthu akhale pfumbi;Nimuti, Bwererani inu, ana a anthu.

4. Pakuti pamaso panu zaka zikwiZikhala ngati dzulo, litapita,Ndi monga ulonda wa usiku.

5. Muwatenga ngati ndi madzi akulu, akhala ngati tulo;Mamawa akhala ngati msipu waphuka.

6. Mamawa uphuka bwino;Madzulo ausenga, nuuma.

7. Pakuti tionongeka mu mkwiyo wanu;Ndipo m'kuzaza kwanu tiopsedwa.

Masalmo 90