26. Iye adzandichula, ndi kuti, Inu ndinu Atate wanga,Mulungu wanga, ndi thanthwe la cipulumutso canga.
27. Inde ndidzamuyesa mwana wanga woyamba,Womveka wa mafumu a pa dziko lapansi.
28. Ndidzamsungira cifundo canga ku nthawi yonse,Ndipo cipangano canga cidzalimbika pa iye.
29. Ndidzakhalitsanso mbeu yace cikhalire,Ndi mpando wacifumu wace ngati masiku a m'mwamba.
30. Ana ace akataya cilamulo canga,Osayenda m'maweruzo anga:
31. Nakaipsa malembo anga;Osasunga malamulo anga;