Masalmo 89:26-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Iye adzandichula, ndi kuti, Inu ndinu Atate wanga,Mulungu wanga, ndi thanthwe la cipulumutso canga.

27. Inde ndidzamuyesa mwana wanga woyamba,Womveka wa mafumu a pa dziko lapansi.

28. Ndidzamsungira cifundo canga ku nthawi yonse,Ndipo cipangano canga cidzalimbika pa iye.

29. Ndidzakhalitsanso mbeu yace cikhalire,Ndi mpando wacifumu wace ngati masiku a m'mwamba.

30. Ana ace akataya cilamulo canga,Osayenda m'maweruzo anga:

31. Nakaipsa malembo anga;Osasunga malamulo anga;

Masalmo 89