Masalmo 88:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Munandiika kunsi kwa dzenje,Kuti mdima, kozama.

7. Mkwiyo wanu utsamira pa ine,Ndipo munandizunza ine ndi mafunde anu onse.

8. Munandisiyanitsira wodziwana nane kutali;Munandiika ndiwakhalire conyansa:Ananditsekereza osakhoza kuturuka ine.

9. Diso langa lapuwala cifukwa ca kuzunzika kwanga:Ndimaitana Inu, Yehova, tsiku lonse;Nditambalitsira manja anga kwa Inu.

10. Kodi mudzacitira akufa zodabwiza?Kodi adzaukanso otisiyawo, ndi kukulemekezani?

11. Adzafotokozera cifundo canu kumanda kodi,Cikhulupiriko canu ku malo a cionongeko?

Masalmo 88