Masalmo 84:9-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Onani, Mulungu, ndinu cikopa cathu;Ndipo penyani pa nkhope ya Wodzozedwa wanu.

10. Pakuti tsiku limodzi m'mabwalo anu likoma koposa masiku ambirimbiri akukhala pena,Kukhala inewapakhomo m'nyumba ya Mulungu wanga,Kundikonda ine koposa kugonera m'mahema a coipa,

11. Pakuti Yehova Mulungu ndiye dzuwa ndi cikopa;Yehova adzapatsa cifundo ndi ulemerero;Sadzakaniza cokoma iwo akuyenda angwiro,

12. Yehova wa makamu,Wodala munthu wakukhulupirira Inu.

Masalmo 84