Masalmo 83:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Mulungu wanga, muwaike akhale ngati mungu;Ngati ziputu zomka ndi mphepo.

14. Monga moto upsereza nkhalango,Ndi monga lawi liyatsa mapiri;

15. Momwemo muwatsate ndi namondwe,Nimuwaopse ndi kabvumvulu wanu.

16. Acititseni manyazi pankhope pao;Kuti afune dzina lanu, Yehova.

Masalmo 83