13. Mulungu wanga, muwaike akhale ngati mungu;Ngati ziputu zomka ndi mphepo.
14. Monga moto upsereza nkhalango,Ndi monga lawi liyatsa mapiri;
15. Momwemo muwatsate ndi namondwe,Nimuwaopse ndi kabvumvulu wanu.
16. Acititseni manyazi pankhope pao;Kuti afune dzina lanu, Yehova.