Masalmo 78:65-68 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

65. Pamenepo Ambuye anauka ngati wam'tulo;Ngati ciphona cakucita nthungululu ndi vinyo.

66. Ndipo anapanda otsutsana naye kumbuyo;Nawapereka akhale otonzeka kosatha.

67. Tero anakana hema wa Yosefe;Ndipo sanasankha pfuko la Efraimu;

68. Koma anasankha pfuko la Yuda,Phiri la Ziyoni limene analikonda.

Masalmo 78