65. Pamenepo Ambuye anauka ngati wam'tulo;Ngati ciphona cakucita nthungululu ndi vinyo.
66. Ndipo anapanda otsutsana naye kumbuyo;Nawapereka akhale otonzeka kosatha.
67. Tero anakana hema wa Yosefe;Ndipo sanasankha pfuko la Efraimu;
68. Koma anasankha pfuko la Yuda,Phiri la Ziyoni limene analikonda.