Masalmo 78:51-57 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

51. Ndipo anapha ana oyamba onse a mu Aigupto,Ndiwo oyamba a mphamvu yao m'mahema a Hamu:

52. Koma anaturutsa anthu ace ngati nkhosa,Nawatsogoza ngati gulu la zoweta m'cipululu.

53. Ndipo anawatsogolera mokhulupirika,Kotero kuti sanaopa;Koma nyanja inamiza adani ao.

54. Ndipo anawafikitsa ku malire a malo ace oyera,Ku phiri ili, dzanja lamanja lace lidaligula.

55. Ndipo anapitikitsa amitundu pamaso pao,Nawagawira colowa cao, ndi muyeso,Nakhalitsa mafuko a Israyeli m'mahema mwao.

56. Koma anamuyesa napikisana ndi Mulungu Wam'mwambamwamba,Osasunga mboni zace;

57. Koma anabwerera m'mbuyo, nacita zosakhulupirika monga makolo ao:Anapatuka ngati uta wolenda,

Masalmo 78