27. Ndipo anawabvumbitsira nyama ngati pfumbi,Ndi mbalame zouluka ngati mcenga wa kunyanja:
28. Ndipo anazigwetsa pakati pa misasa yao,Pozungulira pokhala iwo.
29. Potero anadya nakhuta kwambiri;Ndipo anawapatsa cokhumba iwo.
30. Asanathe naco cokhumba cao,Cakudya cao ciri m'kamwa mwao,
31. Pamenepo mkwiyo wa Mulungu unawaukira,Ndipo anapha mwa onenepa ao,Nagwetsa osankhika a Israyeli.
32. Cingakhale ici conse anacimwanso,Osabvomereza zodabwiza zace.