Masalmo 78:25-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Yense anadya mkate wa omveka:Anawatumizira cakudya cofikira,

26. Anaombetsa m'mwamba mphepo ya kum'mawa:Natsogoza mwela ndi mphamvu yace.

27. Ndipo anawabvumbitsira nyama ngati pfumbi,Ndi mbalame zouluka ngati mcenga wa kunyanja:

28. Ndipo anazigwetsa pakati pa misasa yao,Pozungulira pokhala iwo.

29. Potero anadya nakhuta kwambiri;Ndipo anawapatsa cokhumba iwo.

30. Asanathe naco cokhumba cao,Cakudya cao ciri m'kamwa mwao,

Masalmo 78