21. Cifukwa cace Yehova anamva, nakwiya;Ndipo anayatsa moto pa Yakobo,Ndiponso mkwiyo unakwera pa Israyeli;
22. Popeza sanakhulupirira Mulungu,Osatama cipulumutso cace.
23. Koma analamulira mitambo iri m'mwamba,Natsegula m'makomo a kumwamba.
24. Ndipo anawabvumbitsira mana, adye,Nawapatsa tirigu wa kumwamba.