Masalmo 78:11-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo anaiwala zocita Iye,Ndi zodabwiza zace zimene anawaonetsa.

12. Anacita codabwiza pamaso pa makolo ao,M'dziko la Aigupto ku cidikha ca Zoanu.

13. Anagawa nyanja nawapititsapo;Naimitsa madziwo ngati khoma.

14. Ndipo msana anawatsogolera ndi mtamboNdi usiku wonse ndi kuunika kwa moto.

15. Anang'alula thanthwe m'cipululu,Ndipo anawamwetsa kocuruka monga m'madzi ozama.

16. Anaturukitsa mitsinje m'thanthwe,Inde anatsikitsa madzi ngati mitsinje.

17. Koma anaonjeza kuincimwira Iye,Kupikisana ndi Wam'mwambamwamba m'cipululu.

18. Ndipo anayesa Mulungu mumtimamwaoNdi kupempha cakudya monga mwa kulakalaka kwao.

Masalmo 78