Masalmo 77:12-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo ndidzalingalira nchito yanu yonse,Ndi kulingalirabe zimene munazicita Inu.

13. Mulungu, m'malo opatulika muli njira yanu;Mulungu wamkuru ndani monga Mulungu?

14. Inu ndinu Mulungu wakucita codabwiza;Munazindikiritsa mphamvu yanu mwa mitundu ya anthu.

15. Munaombola anthu anu ndi mkonowanu,Ndiwo ana a Yakobo, ndi a Yosefe.

16. Madziwo anakuonani Mulungu;Anakuonani madziwo; anacita mantha:Zozama zomwe zinanjenjemera,

17. Makongwa anatsanula madzi;Thambo lidamvetsa liu lace;Mibvi yanu yomwe inaturukira.

18. Liu la bingu lanu linatengezanatengezana;Mphezi zinaunikira ponse pali anthu;Dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.

19. Njira yanu inali m'nyanja,Koyenda Inu nku madzi akulu,Ndipo mapazi anu sanadziwika.

Masalmo 77