10. Wotsutsanayo adzatonza kufikira liti, Mulungu?Kodi mdani adzanyoza dzina lanu nthawi yonse?
11. Mubwezeranji dzanja lanu, ndilo dzanja lamanja lanu?Muliturutse ku cifuwa canu ndipo muwatheretu.
12. Koma Mulungu ndiye mfumu yanga kuyambira kale,Wocita zakupulumutsa pakati pa dziko lapansi.
13. Mudagawa nyanja ndi mphamvu yanu;Mudaswa mitu ya zoopsa za m'madzi.