19. Ha! m'kamphindi ayesedwa bwinja;Athedwa konse ndi zoopsya.
20. Monga anthu atauka, apepula loto;Momwemo, Inu Ambuye, pakuuka mudzapeputsa cithunzithunzi cao.
21. Pakuti mtima wanga udawawa,Ndipo ndinalaswa m'imso zanga;
22. Ndinali wam'thengo, wosadziwa kanthu;Ndinali ngati nyama pamaso panu.
23. Koma ndikhala ndi Inu cikhalire:Mwandigwira dzanja langa la manja.