Masalmo 73:17-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Mpaka ndinalowa m'zoyera za Mulungu,Ndi kulingalira citsiriziro cao.

18. Indedi muwaika poterera:Muwagwetsa kuti muwaononge.

19. Ha! m'kamphindi ayesedwa bwinja;Athedwa konse ndi zoopsya.

20. Monga anthu atauka, apepula loto;Momwemo, Inu Ambuye, pakuuka mudzapeputsa cithunzithunzi cao.

21. Pakuti mtima wanga udawawa,Ndipo ndinalaswa m'imso zanga;

22. Ndinali wam'thengo, wosadziwa kanthu;Ndinali ngati nyama pamaso panu.

23. Koma ndikhala ndi Inu cikhalire:Mwandigwira dzanja langa la manja.

24. Mudzanditsogolera ndi uphungu wanu,Ndipo mutatero, mudzandilandira m'ulemerero,

Masalmo 73