Masalmo 72:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Masiku ace wolungama adzakhazikika;Ndi mtendere wocuruka, kufikira sipadzakhala mwezi.

8. Ndipo adzacita ufumu kucokera kunyanja kufikira kunyanja,Ndi kucokera ku Mtsinje kufikira malekezero a dziko lapansi.

9. Okhala m'cipululu adzagwadira pamaso pace;Ndi adani ace adzaluma nthaka.

10. Mafumu a ku Tarisi ndi ku Zisumbuzo adzabwera naco copereka;Mafumu a ku Sheba ndi Seba adzadza nazo mphatso,

11. Inde mafumu onse adzamgwadira iye:Amitundu onse adzamtumikira.

12. Pakuti adzapulumutsa waumphawi wopfuulayo;Ndi wozunzika amene alibe mthandizi.

Masalmo 72