6. Adzanga mvula yakugwa pa udzu wosenga:Monga mvula yothirira dziko.
7. Masiku ace wolungama adzakhazikika;Ndi mtendere wocuruka, kufikira sipadzakhala mwezi.
8. Ndipo adzacita ufumu kucokera kunyanja kufikira kunyanja,Ndi kucokera ku Mtsinje kufikira malekezero a dziko lapansi.
9. Okhala m'cipululu adzagwadira pamaso pace;Ndi adani ace adzaluma nthaka.