Masalmo 72:6-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Adzanga mvula yakugwa pa udzu wosenga:Monga mvula yothirira dziko.

7. Masiku ace wolungama adzakhazikika;Ndi mtendere wocuruka, kufikira sipadzakhala mwezi.

8. Ndipo adzacita ufumu kucokera kunyanja kufikira kunyanja,Ndi kucokera ku Mtsinje kufikira malekezero a dziko lapansi.

9. Okhala m'cipululu adzagwadira pamaso pace;Ndi adani ace adzaluma nthaka.

Masalmo 72