Masalmo 69:9-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Pakuti cangu ca pa nyumba yanu candidya;Ndi zotonza za iwo otonza Inu zandigwera ine.

10. Ndipo ndinalira pa kusala kwa moyo wanga,Koma uku kunandikhalira cotonza.

11. Ndipo cobvala canga ndinayesa ciguduli,Koma amandiphera mwambi.

12. Okhala pacipata akamba za ine; Ndipo oledzera andiyimba.

13. Koma ine, pemphero langa liri kwa Inu, Yehova, m'nyengo yolandirika;Mulungu, mwa cifundo canu cacikuru,Mundibvomereze ndi coonadi ca cipulumutso canu.

14. Mundilanditse kuthope, ndisamiremo:Ndilanditseni kwa iwo akundida, ndi kwa madzi ozama.

15. Cigumula cisandifotsere,Ndipo cakuya cisandimize;Ndipo asanditsekere pakamwa pace pa dzenje.

16. Mundiyankhe Yehova; pakuti cifundo canu ncokoma;Munditembenukire monga mwa unyinji wa nsoni zokoma zanu.

17. Ndipo musabisire nkhope yanu mtumiki wanu;Pakuti ndisautsika ine; mundiyankhe msanga.

18. Yandikizani moyo wanga, ndi kuuombola;Ndipulumutseni cifukwa ca adani anga,

19. Mudziwa cotonza canga, ndi manyazi anga, ndi cimpepulo canga:Akundisautsa ali pamaso panu,

20. Cotonza candiswera mtima, ndipo ndidwala ine;Ndipo ndinayembekeza wina wondicitira cifundo, koma palibe;Ndinayembekeza onditonthoza mtima, osawapeza.

21. Ndipo anandipatsa ndulu ikhale cakudya canga;Nandimwetsa vinyo wosasa pomva ludzu ine.

22. Gome lao likhale msampha pamaso pao;Pokhala ndi mtendere iwo, likhale khwekhwe.

23. M'maso mwao mude, kuti asapenye;Ndipo munjenjemeretse m'cuuno mwao kosalekeza.

Masalmo 69