Masalmo 66:7-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Acita ufumu mwa mphamvu yace kosatha;Maso ace ayang'anira amitundu;Opikisana ndi Iye asadzikuze.

8. Lemekezani Mulungu wathu, mitundu ya anthu inu,Ndipo mumveketse liu la cilemekezo cace:

9. Iye amene asunga moyo wathu tingafe,Osalola phazi lathu literereke.

10. Pakati munatiyesera, Mulungu:Munatiyenga monga ayenga siliya.

11. Munapita nafe kuukonde;Munatisenza cothodwetsa pamsana pathu.

12. Munapititsa anthu oberekeka pamwamba pamitu pathu;Tinapyola moto ndi madzi; Koma munatifikitsa potitsitsimutsa.

13. Ndidzalowa m'nyumba yanu ndi nsembe zopsereza,Ndidzakucitirani zowinda zanga,

14. Zimene inazichula milomo yanga,Ndinazinena pakamwa panga pasautsika ine.

Masalmo 66