Masalmo 62:9-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Indetu, anthu acabe ndi mpweya, ndipo anthu akuru ndi bodza:Pakuwayesa apepuka;Onse pamodzi apepuka koposa mpweya,

10. Musakhulupirire kusautsa, ndipo musatama cifwamba;Cikacuruka cuma musakhazikepo mitima yanu.

11. Mulungu ananena kamodzi, ndinacimva kawiri:Kuti mphamvu ndi yace ya Mulungu:

12. Cifundonso ndi canu, Ambuye:Cifukwa Inu musudzula munthu ali yense monga mwa nchito yace.

Masalmo 62