5. Mantha ndi kunjenjemera zandidzera,Ndipo zoopsetsa zandikuta.
6. Ndipo ndinati, Ha, wina akadandipatsa mapiko onga a njiwaMwenzi nditauluka, ndi kukhaliratu.
7. Onani, ndikadathawira kutari,Ndikadagona m'cipululu.
8. Ndikadafulumira ndipulumukeKu mphepo yolimba ndi namondwe.