7. Koma Inu munatipulumutsa kwa iwo akutsutsana nafe,Ndipo akudana nafe, mudawacititsa manyazi.
8. Mwa Mulungu tidzitamanda tsiku lonse,Ndipo dzina lanu tidzaliyamika kosatha.
9. Koma mwatitaya, ndi kutinyazitsa;Ndipo simuturuka nao makamu a nkhondo athu.
10. Mutibwereretsa kuthawa otisautsa:Ndipo akudana nafe adzifunkhira okha.
11. Mwatipereka ngati nkhosa zoyenera kuzidya;Ndipo mwatibalalitsa mwa amitundu.