Masalmo 44:21-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Mulungu sakadasanthula ici kodi?Pakuti adziwa zinsinsi za mtima.

22. Koma, cifukwa ca Inu, tiphedwa tsiku lonse;Tiyesedwa ngati nkhosa zakuzipha.

23. Galamukani, mugoneranji, Ambuye?Ukani, musatitaye citayire.

24. Mubisiranji nkhope yanu,Ndi kuiwala kuzunzika ndi kupsinjika kwathu?

25. Pakuti moyo wathu waweramira kupfumbi:Pamimba pathu pakangamira dziko lapansi.

26. Ukani, tithandizeni,Tiomboleni mwa cifundo canu.

Masalmo 44