21. Mulungu sakadasanthula ici kodi?Pakuti adziwa zinsinsi za mtima.
22. Koma, cifukwa ca Inu, tiphedwa tsiku lonse;Tiyesedwa ngati nkhosa zakuzipha.
23. Galamukani, mugoneranji, Ambuye?Ukani, musatitaye citayire.
24. Mubisiranji nkhope yanu,Ndi kuiwala kuzunzika ndi kupsinjika kwathu?
25. Pakuti moyo wathu waweramira kupfumbi:Pamimba pathu pakangamira dziko lapansi.
26. Ukani, tithandizeni,Tiomboleni mwa cifundo canu.