4. Wodala munthuyo wakuyesa Yehova wokhulupirika;Wosasamala odzikuza, ndi opatukira kubodza.
5. Inu, Yehova, Mulungu wanga, zodabwiza zanu mudazicita nzambiri,Ndipo zolingirira zanu za pa ife;Palibe wina wozifotokozera Inu;Ndikazisimba ndi kuzichula, Zindicurukira kuziwerenga.
6. Nsembe ndi copereka simukondwera nazo;Mwanditsegula makutu:Nsembe yopsereza ndi yamacimo simunapempha.
7. Pamenepo ndinati, Taonani, ndadza;M'buku mwalembedwa za Ine:
8. Kucita cikondwero canu kundikonda, Mulungu wanga;Ndipo malamulo anu ali m'kati mwamtima mwanga.