Masalmo 37:10-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Katsala kanthawi ndipo woipa adzatha psiti:Inde, udzayang'anira mbuto yace, nudzapeza palibe.

11. Koma ofatsa adzalandira dziko lapansi;Nadzakondwera nao mtendere wocuruka.

12. Woipa apangira ciwembu wolungama,Namkukutira mano.

13. Ambuye adzamseka:Popeza apenya kuti tsiku lace likudza.

14. Oipa anasolola lupanga, nakoka uta wao;Alikhe ozunzika ndi aumphawi,Aphe amene ali oongoka m'njira:

15. Lupanga lao lidzalowa m'mtima mwao momwe,Ndipo mauta ao adzatyoledwa.

16. Zocepa zace za wolungama zikomaKoposa kucuruka kwao kwa oipa ambiri.

17. Pakuti manja a oipa adzatyoledwa:Koma Yehova acirikiza olungama.

18. Yehova adziwa masiku a anthu angwiro:Ndipo cosiyira cao cidzakhala cosatha.

19. Sadzacita manyazi m'nyengo yoipa:Ndipo m'masiku a njala adzakhuta.

Masalmo 37