Masalmo 33:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. M'malo akhalamo Iye, amapenya pansiPa onse akukhala m'dziko lapansi;

15. Iye amene akonza mitima ya iwo onse,Amene azindikira zocita zao zonse.

16. Palibe mfumu yoti gulu lalikuru limpulumutsa:Mphamvu yaikuru siicilanditsa ciphona,

17. Kavalo safikana kupulumuka naye:Cinkana mphamvu yace njaikuru sapulumutsa.

18. Taonani, diso la Yehova liri pa iwo akumuopa Iye,Pa iwo akuyembekeza cifundo cace;

19. Kupulumutsa moyo wao kwa imfa,Ndi kuwasunga ndi moyo m'nyengo ya njala.

20. Moyo wathu walindira Yehova:Iye ndiye thandizo lathu ndi cikopa cathu.

Masalmo 33