Masalmo 31:12-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndaiwalika m'mtima monga wakufa:Ndikhala monga cotengera cosweka.

13. Pakuti ndamva ugogodi wa ambiri,Mantha andizinga:Pondipangira ciwembu,Anatsimikiza mtima kulanda moyo wanga.

14. Koma ine ndakhulupirira Inu, Yehova:Ndinati, Inu ndinu Mulungu wanga,

15. Nyengo zanga ziri m'manja mwanu:Mundilanditse m'manja a adani anga, ndi kwa iwo akundilondola ine.

Masalmo 31