5. Liu la Yehova lithyola mitengo yamkungudza;Inde Yehova athyola mikungudza ya ku Lebano.
6. Aitumphitsa monga mwana wa ng'ombe;Lebano ndi Sirio monga msona wa njati.
7. Liu la Yehova ligawa malawi a moto.
8. Liu la Yehova ligwedeza cipululu;Yehova agwedeza cipululu ca Kadese.