Masalmo 22:18-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Agawana zobvala zanga,Nalota maere pa malaya anga,

19. Koma Inu, Yehova, musakhale kutari;Mphamvu yanga Inu, mufulumire kundithandiza.

20. Landitsani moyo wanga kulupanga;Wokondedwa wanga ku mphamvu ya garu,

21. Ndipulumutseni m'kamwa mwa mkango;Inde mwandiyankha ine ndiri pa nyanga za njati,

22. Ndidzalalikira dzina lanu kwa abale anga:Pakati pa msonkhano ndidzakulemekezani.

23. Inu akuopa Yehova, mumlemekeze;Inu nonse mbumba ya Yakobo, mumcitire ulemu;Ndipo mucite mantha ndi Iye, inu nonse mbumba ya Israyeli.

24. Pakuti sanapeputsa ndipo sananyansidwa ndi zunzo la wozunzika;Ndipo sanambisira nkhope yace;Koma pompfuulira Iye, anamva.

25. Lemekezo langa lidzakhala la Inu mu msonkhano waukuru:Zowinda zanga ndidzazicita pamaso pa iwo akumuopa Iye.

26. Ozunzika adzadya nadzakhuta:Adzayamika Yehova iwo amene amfuna:Ukhale moyo mtima wako nthawi zonse.

Masalmo 22