6. Anazikhazikanso ku nthawi za nthawi;Anazipatsa cilamulo cosatumphika.
7. Lemekezani Yehova kocokera ku dziko lapansi,Zinsomba inu, ndi malo ozama onse;
8. Moto ndi matalala, cipale cofewa ndi nkhungu;Mphepo ya namondwe, yakucita mau ace;
9. Mapiri ndi zitunda zonse;Mitengo yazipatso ndi yamikungudza yonse: