14. Yehova agwiriziza onse akugwa,Naongoletsa onse owerama.
15. Maso a onse ayembekeza Inu;Ndipo muwapatsa cakudya cao m'nyengo zao.
16. Muniowetsa dzanja lanu,Nimukwaniritsira zamoyo zonse cokhumba cao.
17. Yehova ali wolungama m'njira zace zonse,Ndi wacifundo m'nchito zace zonse.