12. Kudziwitsa ana a anthu zamphamvu zace,Ndi ulemerero waukuru wa ufumu wace.
13. Ufumu wanu ndiwo ufumu womka muyaya,Ndi kuweruza kwanu kufikira mibadwo yonse yonse.
14. Yehova agwiriziza onse akugwa,Naongoletsa onse owerama.
15. Maso a onse ayembekeza Inu;Ndipo muwapatsa cakudya cao m'nyengo zao.
16. Muniowetsa dzanja lanu,Nimukwaniritsira zamoyo zonse cokhumba cao.