Masalmo 145:12-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Kudziwitsa ana a anthu zamphamvu zace,Ndi ulemerero waukuru wa ufumu wace.

13. Ufumu wanu ndiwo ufumu womka muyaya,Ndi kuweruza kwanu kufikira mibadwo yonse yonse.

14. Yehova agwiriziza onse akugwa,Naongoletsa onse owerama.

15. Maso a onse ayembekeza Inu;Ndipo muwapatsa cakudya cao m'nyengo zao.

16. Muniowetsa dzanja lanu,Nimukwaniritsira zamoyo zonse cokhumba cao.

Masalmo 145