Masalmo 139:6-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Kudziwa ici kundilaka ndi kundidabwiza:Kundikhalira patali, sindifikirako.

7. Ndidzapita kuti kuzembera mzimu wanu?Kapena ndidzathawira kuti kuzembera nkhope yanu?

8. Ndikakwera kumka kumwamba, muli komweko;Kapena ndikadziyalira ku Gehena, taonani, muli komweko.

9. Ndikadzitengera mapiko a mbanda kuca,Ndi kukhala ku malekezero a nyanja;

10. Kungakhale komweko dzanja lanu lidzanditsogolera,Nilidzandigwira dzanja lanu lamanja.

11. Ndipo ndikati, Koma mdima undiphimbe,Ndi kuunika kondizinga kukhale usiku:

12. Ungakhale mdima sudetsa pamaso panu,Koma usiku uwala ngati usana:Mdima ukunga kuunika.

13. Pakuti Inu munalenga imso zanga;Munandiumba ndisanabadwe ine.

14. Ndikuyamikani cifukwa kuti cipangidwe canga ncoopsa ndi codabwiza;Nchito zanu nzodabwiza;Moyo wanga ucidziwa ici bwino ndithu.

Masalmo 139