Masalmo 139:10-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Kungakhale komweko dzanja lanu lidzanditsogolera,Nilidzandigwira dzanja lanu lamanja.

11. Ndipo ndikati, Koma mdima undiphimbe,Ndi kuunika kondizinga kukhale usiku:

12. Ungakhale mdima sudetsa pamaso panu,Koma usiku uwala ngati usana:Mdima ukunga kuunika.

13. Pakuti Inu munalenga imso zanga;Munandiumba ndisanabadwe ine.

Masalmo 139