Masalmo 132:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ngati ndidzalola maso anga agone,Kapena zikope zanga ziodzere;

5. Kufikira nditapezera Yehova malo,Cokhalamo Wamphamvuyo wa Yakobo?

6. Taonani, tinacimva m'Efrata;Tinacipeza ku cidikha ca kunkhalango.

7. Tidzalowa mokhalamo Iye;Tidzagwadira ku mpando wa mapazi ace.

8. Ukani, Yehova, lowani ku mpumulo wanu;Inu ndi hema wa mphamvu yanu,

9. Ansembe anu abvale cilungamo;Ndi okondedwa anu apfuule mokondwera.

10. Cifukwa ca Davide mtumiki wanuMusabweze nkhope ya wodzozedwa wanu.

11. Yehova analumbira Davide zoona;Sadzalibweza; ndi kuti,Wa iwo okhala zipatso za thupi lako ndidzaika pa mpando wacifumu wako.

Masalmo 132