Masalmo 119:88-95 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

88. Mundipatse moyo monga mwa cifundo canu;Ndipo ndidzasamalira mboni ya pakamwa panu,

89. Mau anu aikika kumwamba,Kosatha, Yehova.

90. Cikhulupiriko canu cifikira mibadwo mibadwo;Munakhazikitsa dziko lapansi, ndipo likhalitsa.

91. Kunena za maweruzo anu alimbikira kufikira lero;Pakuti onsewa ndiwo atumiki anu.

92. Cilamulo canu cikadapanda kukhala cikondweretso canga,Ndikadatayika m'kuzunzika kwanga.

93. Sindidzaiwala malangizo anu nthawi zonse;Popeza munandipatsa nao moyo.

94. Ine ndine wanu, ndipulumutseniPakuti ndinafuna malangizo anu.

95. Oipa anandilalira kundiononga;Koma ndizindikira mboni zanu.

Masalmo 119