68. Inu ndinu wabwino, ndi wakucita zabwino;Mundiphunzitse malemba anu.
69. Odzikuza anandipangira bodza:Ndidzasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70. Mtima wao unona ngati mafuta;Koma ine ndikondwera naco cilamulo canu.
71. Kundikomera kuti ndinazunzidwa;Kuti ndiphunzire malemba anu.