Masalmo 119:30-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Ndinasankha njira yokhulupirika;Ndinaika maweruzo anu pamaso, panga,

31. Ndimamatika nazo mboni zanu;Musandicititse manyazi, Yehova.

32. Ndidzathamangira njira ya malamulo anu,Mutakulitsa mtima wanga.

33. Mundiphunzitse, Yehova, njira ya malemba anu;Ndidzaisunga kufikira kutha kwace.

34. Mundizindikiritse, ndipo ndidzasunga malamulo anu;Ndidzawasamalira ndi mtima wanga wonse.

35. Mundiyendetse mopita malamulo anu;Pakuti ndikondwera m'menemo.

36. Lingitsani mtima wanga ku mboni zanu,Si ku cisiriro ai.

Masalmo 119